fbpx

Play Football Malawi

Bungwe la Play Football Malawi, limakhazikitsa malo a za masewero ndi maphuninziro ku Malawi, Cholinga chachikulu ndikuthandiza ana a ku Malawi powapatsa danga ndi kuwafikira mumagawo awa:

Icon_Bildung
Maphunziro

Kudzera mu maphunzira, ana azindikira kuthekera kwao.
Mwana aliyense ali ndi ufulu wa maphunziro.

Icon_Nahrung
Chakudya

Chakudya chamagawo onse ndi chofunikira ku moyo wa thanzi wa mwana.

Icon_Sport
Masewero

Timaphunzira zambiri kudzera mu masewero.
Kupyolera ku masewero ampira wa miyendo tikufikira ana ochuluka.

Timalimbikitsa ana powathandiza kuti azindikire kuthekera kumene ali nako popanga zinthu zokhazikika zomwe zingasinthe miyoyo yawo, ya banja lawo komanso mudzi wawo. Kuti tikwaniritse izi, timatsindika pa kulumikizana ndi kugwilira ntchito limodzi ndi anzathu.

Dziwani zambiri poyang’ana pa tsamba lathu la intaneti: Play Football Malawi Website    FAQ

Ku Maphunziro

Ku Malawi, si chachilendo kuona zithunzi za ana osachepera 100 atakhala pansi mkalasi lophunziliramo. Ambiri a anawa amakhalanso kuti alibe zipangizo zophunzilira ngati zolembera ndi polembapo. Ana ochulukanso alibe mwayi wa sukulu. Zikomo Foundation, ndi ma bungwe ena alowelerapo ndi kuyamba kumanga malo ophunzilirapo ndi kupereka zipangizo zophunzitsira ndi kuphunzilira.

Dziwani za mbiri

 

Ndende ya a Chinyamata

Ndende ya a chinyamata nthawi zambiri imakhala yothithikana. Kusowekera kwa chakudya cha magulu, ukhondo ndi malo abwino ogona zimapangitsa kuti matenda achulukire ku maloku. a Zikomo Foundation timathandizira akayidi kuti apeze ma phunziro, chakudya choonjezera pa chomwe amadya, masewero olimbitsa thupi, komanso mankhwala osiyanasiyana.

Dziwani za mbiri

Thandinzo kwa ana a masiye

Ku Malawi kuli ana amasiye ochuluka chifukwa cha kusoweka kwa umoyo wa thanzi, matenda a HIV/AIDS komanso kuchuluka kwa imfa za amayi panthawi ya kubereka kwao. a Crisis Nursery ali ndi nyumba imene amasungira ndikulelera ana amene mayi wawo wamwalira pa nthawi ya kubadwa kwao kufikira nthawi imene banja la kwao lingadzatenge udindo wa kuwalera. Zikomo Foundation imathandiza kumeneku m’magawo a ndalama, chakudya komanso zoseweretsa ana. Kulowelerapo kwathu, kumapereka kuthekera kwa Crisis Nursery kuti akwanitse ku samala ndi kulera ana ochuluka amene alibe mayi.

Dziwani za mbiri

Thandizo ku chipatala cha ana

Chipatala cha Kamuzu Central ndicho chachikulu mu chigawo chapakati ku Malawi ndipo chimakhala chikuthandiza anthu ochuluka zomwe zimapangitsa kuti afune chithandizo chochuluka. mavuto  alipo ochuluka ndipo Zikomo Foundation ikuthandiza magawo a chakudya, ukhondo ndi zina.

Dziwani za mbiri

Thandizo kwa anthu osowa ndi okalamba

Umphawi wa ku ukalamba ndi waukulu kwambiri ku Malawi chifukwa kulibe ndondomeko zokhazikika zabwino zothandizira anthu omwe apuma pa ntchito kuchokera ku boma komanso mabungwe. Zikomo Foundation imagawa maphukusi athandizo mwezi uliwonse zomwe zimathandiza pa zofuna zawo za tsiku ndi tsiku ku Likuni kumene kuli sukulu yathu ya masewero a mpira wa miyendo.

Dziwani za mbiri

Ntchito zina

projekte_kredite
Ngongole

Kupititsa patsogolo a malondo ang’onoang’ono timapangitsa kuti umoyo wa anthu utukuke ndi kupita patsogolo. Timathandiza anthu kukhazikitsa ndi kupititsa patsogolo malando awo powapatsa maphunziro komanso ngongole.

field
Ulimi

Alimi osachepera 750 million ku Africa alibe maphunziro ndi ukadaulo wa za ulimi zomwe zimapangitsa kuti asamapeze phindu mu ulimi wawo. Zikomo Foundation ikupanga ulimi wamakono molumikizana ndi alimi a m’midzi.

House
Zomangamanga

Zikomo Foundation ikulimbikitsa chitukuko cha zomangamanga. Nyumba zokhalamo ndi zogwilira ntchito ndi zokhumbika ku Malawi. Bungweli kudzera ku malo ake likhazikitsa nyumba, zokhalamo anthu komanso zogwilira ntchito.